Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Numeri 32:6 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno?

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

6 Ndipo Mose anati kwa ana a Gadi ndi ana a Rubeni, Kodi abale anu apite kunkhondo, ndi inu mukhale pansi kuno?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Ndipo Mose anati kwa ana a Gadi ndi ana a Rubeni, Kodi abale anu apite kunkhondo, ndi inu mukhale pansi kuno?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Koma Mose adafunsa ana a Gadi ndi ana a Rubeni kuti, “Kodi abale anu azikamenya nkhondo, inu mutangokhala kuno?

Onani mutuwo Koperani




Numeri 32:6
6 Mawu Ofanana  

Uriya anayankha Davide kuti, “Bokosi la Chipangano ndi Israeli ndiponso Yuda akukhala mʼmatenti, ndipo mbuye wanga Yowabu ndi ankhondo anu mbuye wanga amanga misasa pa mtetete. Ine ndingapite bwanji ku nyumba yanga kukadya ndi kumwa ndiponso kugona ndi mkazi wanga? Pali inu wamoyo, ine sindidzachita chinthu chimenechi.”


Iwo anati, ‘Ngati tapeza ufulu pamaso panu atumiki anufe, mutipatse dziko limeneli kuti likhale lathu. Tisawoloke nanu Yorodani.’ ”


Chifukwa chiyani mukufowoketsa Aisraeli kupita mʼdziko limene Yehova wawapatsa?


Chikondi chilibe mwano, sichodzikonda, sichipsa mtima msanga, sichisunga mangawa.


Musamangofuna zokomera inu nokha koma aliyense azifuna zokomeranso ena.


Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera zitoliro zoyitanira nkhosa? Pakati pa anthu a fuko la Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa