Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Numeri 27:4 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Nʼchifukwa chiyani dzina la abambo athu lasowa pakati pa fuko lawo, kodi popeza analibe mwana wamwamuna? Tipatseni cholowa chathu pakati pa abale a abambo athu.”

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

4 Lichotsedwerenji dzina la atate wathu pakati pa banja lake, popeza alibe mwana wamwamuna? Tipatseni dziko lathulathu pakati pa abale a atate wathu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Lichotsedwerenji dzina la atate wathu pakati pa banja lake, popeza alibe mwana wamwamuna? Tipatseni dziko lathulathu pakati pa abale a atate wathu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 Kodi dzina la bambo wathu life chifukwa choti analibe mwana wamwamuna? Mutipatse choloŵa chathu pakati pa abale a bambo wathu.”

Onani mutuwo Koperani




Numeri 27:4
6 Mawu Ofanana  

Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.


Koma Mose anapempha chifundo cha Mulungu wake ndipo anati, “Chonde Yehova, chifukwa chiyani mwakwiyira anthu awa amene munawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.


Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.


“Abambo athu anafera mʼchipululu koma sanali nawo mʼgulu la anthu otsatira Kora, omwe anasonkhana pamodzi kutsutsana ndi Yehova. Abambo athuwo anafa chifukwa cha tchimo lawo ndipo sanasiye ana aamuna.


Tsono Mose anabweretsa nkhani yawo pamaso pa Yehova


Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa