Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Numeri 24:5 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 “Matenti ako ndi okongola kwambiri iwe Yakobo, misasa yako, iwe Israeli!

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

5 Ha? Mahema ako ngokoma, Yakobo; zokhalamo zako, Israele!

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Ha? Mahema ako ngokoma, Yakobo; zokhalamo zako, Israele!

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Mahema ako, iwe Yakobe, nyumba zako, iwe Israele, si kukoma kwake!

Onani mutuwo Koperani




Numeri 24:5
13 Mawu Ofanana  

Paja iwowa sanawachingamire Aisraeli kukawapatsa chakudya ndi madzi. Mʼmalo mwake analemba ganyu Baalamu kuti adzawatemberere. Komabe Mulungu wathu anasandutsa tembererolo kukhala mdalitso.


Moyo wanga ukulakalaka, mpaka kukomoka, kufuna mabwalo a Yehova; Mtima wanga ndi thupi langa zikufuwulira Mulungu wamoyo.


Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi:


Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga; palibe chilema pa iwe.


Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza, wokongola kwambiri ngati Yerusalemu, ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.


Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa


Ndipo wina aliyense wochita zimenezi, kaya munthuyo ndi wotani, Yehova amuchotse ku banja la Yakobo, ngakhale atabweretsa zopereka kwa Yehova Wamphamvuzonse.


Choncho Aisraeli anachita zonse zomwe Yehova analamulira Mose. Umo ndi momwe amamangira misasa yawo pamene panali mbendera zawo, ndipo ankasamuka monga mwa mafuko a makolo awo.


Balaamu atayangʼana, anaona Aisraeli atamanga misasa yawo fuko ndi fuko. Pamenepo mzimu wa Mulungu unabwera pa iye


uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu, yemwe amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse, yemwe amagwa chafufumimba, koma maso ake ali chipenyere:


“Monga zigwa zotambalala, monga minda mʼmbali mwa mtsinje, monga aloe wodzalidwa ndi Yehova, monga mikungudza mʼmbali mwa madzi.


Iwe Israeli, ndiwe wodala! Wofanana nanu ndani anthu opulumutsidwa ndi Yehova? Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu ndi lupanga lanu la ulemerero. Adani ako adzakugonjera, ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”


Koma ine sindinamvere Balaamu, kotero iye anakudalitsani mowirikiza ndipo ndinakulanditsani mʼdzanja lake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa