Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Numeri 23:2 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo awiriwo anapereka ngʼombe imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

2 Ndipo Balaki anachita monga Balamu ananena; ndipo Balaki ndi Balamu anapereka paguwa la nsembe lililonse ng'ombe ndi nkhosa yamphongo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

2 Ndipo Balaki anachita monga Balamu ananena; ndipo Balaki ndi Balamu anapereka pa guwa la nsembe lililonse ng'ombe ndi nkhosa yamphongo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

2 Balaki adachitadi monga momwe adamuuzira Balamu. Ndipo Balaki pamodzi ndi Balamu adapereka ng'ombe yamphongo ndi nkhosa yamphongo pa guwa lililonse.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 23:2
6 Mawu Ofanana  

Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.


Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano, ndipo mukonzenso ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”


Tsono anamutengera ku munda wa Zofimu pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo kumeneko anamanga maguwa ansembe asanu ndi awiri ndipo anapereka nsembe ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.


Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano ndipo mundikonzere ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”


Kenaka Balaamu anati kwa Balaki, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu ineyo ndipite pambali. Mwina Yehova adzabwera kuti akumane nane. Chilichonse chimene akandionetse ndidzakuwuzani” Choncho anapita ku malo okwera a chipululu.


Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo anapereka nsembe ngʼombe imodzi yayimuna ndi nkhosa imodzi yayimuna pa guwa lililonse.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa