Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Numeri 17:7 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

7 Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

7 Ndipo Mose anaika ndodozo pamaso pa Yehova m'chihema cha mboni.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

7 Ndipo Mose anaika ndodozo pamaso pa Yehova m'chihema cha mboni.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

7 Mose adakaziika ndodozo pamaso pa Chauta m'chihema chaumboni.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 17:7
9 Mawu Ofanana  

Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi:


Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.


Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”


Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano.


Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe.


Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo.


Ubweretse Alevi, abale ako, kuchokera ku fuko la abambo ako kuti azikhala ndi iwe ndi kumakuthandiza pamodzi ndi ana ako amuna pamene mukutumikira mu tenti ya umboni.


Pa tsiku limene anayimika chihema, tenti ya umboni, mtambo unaphimba chihemacho. Kuyambira madzulo mpaka mmawa, mtambo umene unali pamwamba pa chihemacho unkaoneka ngati moto.


“Makolo athu anali ndi tenti ya msonkhano pakati pawo mʼchipululu. Anayipanga monga momwe Mulungu anawuzira Mose, molingana ndi chithunzi chimene Mose anachiona.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa