Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Numeri 14:4 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

4 Ndipo anati wina ndi mnzake, Tiike mtsogoleri, tibwerere ku Ejipito.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Ndipo anati wina ndi mnzake, Tiike mtsogoleri, tibwerere ku Ejipito.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 Ndipo adayamba kuuzana kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri kuti tibwerere ku Ejipito.”

Onani mutuwo Koperani




Numeri 14:4
11 Mawu Ofanana  

ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’


koma mwezi wonse, mpaka itakukolani ndi kutopa nayo chifukwa mwakana Yehova yemwe ali pakati panu ndipo mwalira pamaso pake kuti, ‘Bwanji tinachoka ku Igupto?’ ”


Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo.


Kumbukirani mkazi wa Loti!


“Koma makolo athu anakana kumumvera iye. Iwo anamukana iye ndipo mʼmitima mwawo anatembenukira ku Igupto.


Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.”


Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.


Akanakhala kuti akuganizira za dziko limene analisiya akanapeza mpata obwerera kwawo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa