Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Numeri 14:1 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

1 Pamenepo khamu lonse linakweza mau ao, nafuula; ndipo anthuwo analira usikuwo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Pamenepo khamu lonse linakweza mau ao, nafuula; ndipo anthuwo analira usikuwo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Pamenepo mpingo wonse udafuula kwambiri, ndipo anthu adalira usiku umenewo.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 14:1
13 Mawu Ofanana  

Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.


Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.


Farao atalola anthu aja kuti atuluke, Mulungu sanawadzeretse njira yodutsa dziko la Afilisti, ngakhale kuti inali yachidule popeza Mulungu anati, “Ngati anthuwa atadzakumana ndi nkhondo angadzakhumudwe ndi kubwerera ku Igupto.”


Anthu atamva mawu owopsawa, anayamba kulira ndipo palibe anavala zodzikometsera.


kuchokera ku fuko la Aseri, Seturi mwana wa Mikayeli;


Kumeneko tinaona Anefili (ana a Aanaki ochokera kwa Nefili). Ifeyo timangodziona ngati ziwala mʼmaso mwawo, ndipo kwa iwo timaonekadi motero ndithu.”


Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno!


Koma inu simunafune kupitako ndipo munawukira lamulo la Yehova Mulungu wanu.


Munabwererako mukulira pamaso pa Yehova, koma Iye sanalabadire kulira kwanuko ndipo sanakumvetsereni.


Ndipo Yehova atakutulutsani ku Kadesi Barinea anati, “Pitani mukatenge dziko limene ndakupatsani.” Koma munawukira ulamuliro wa Yehova Mulungu wanu. Inu simunamukhulupirire kapena kumumvera.


Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.


Kotero Davide ndi anthu ake analira mofuwula mpaka analibenso mphamvu zolirira.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa