Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Numeri 13:8 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

8 kuchokera ku fuko la Efereimu, Hoseya mwana wa Nuni;

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

8 Wa fuko la Efuremu, Hoseya mwana wa Nuni.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

8 Wa fuko la Efuremu, Hoseya mwana wa Nuni.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

8 M'fuko la Efuremu, adatuma Hoseya mwana wa Nuni.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 13:8
18 Mawu Ofanana  

Ndipo anayamba ulendo wopita ku phiri la Mulungu pamodzi ndi womuthandiza wake Yoswa.


Pamene Yoswa anamva phokoso la anthu anati kwa Mose, “Ku msasa kuli phokoso la nkhondo.”


Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Mose kuyambira ubwana wake, anayankha kuti, “Mbuye wanga Mose, aletseni!”


Amenewa ndiwo mayina a anthu amene Mose anawatuma kukazonda dzikolo. (Hoseya mwana wa Nuni, Mose anamupatsa dzina loti Yoswa).


kuchokera ku fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe;


kuchokera ku fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu;


Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.


Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”


Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.


Tsono Yoswa, mwana wa Nuni anadzazidwa ndi mzimu wanzeru chifukwa nʼkuti Mose atamusanjika manja. Choncho Aisraeli anamumvera ndipo anachita zomwe Yehova analamula Mose.


Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.


Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa