Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Numeri 1:47 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

47 Koma Alevi monga mwa fuko la makolo ao sanawerengedwe mwa iwo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

47 Koma Alevi monga mwa fuko la makolo ao sanawerengedwe mwa iwo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

47 Alevi okha sadaŵaŵerengere kumodzi ndi enawo, potsata banja la makolo ao,

Onani mutuwo Koperani




Numeri 1:47
12 Mawu Ofanana  

Koma Yowabu sanaphatikizepo fuko la Levi ndi fuko la Benjamini pa chiwerengerochi, pakuti lamulo la mfumu linamuyipira.


Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.


Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,


Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.


Koma Alevi sanawawerenge pamodzi ndi Aisraeli enawo monga momwe Yehova analamulira Mose.


Iyi ndi mbiri ya banja la Aaroni ndi Mose pa nthawi yomwe Yehova anayankhula ndi Mose pa phiri la Sinai.


Yehova anawuza Mose mʼchipululu cha Sinai kuti,


“Werenga Alevi monga mwa mabanja awo ndi mafuko awo. Werenga mwamuna aliyense kuyambira wa mwezi umodzi kapena kupitirirapo.”


Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa