Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 69:3 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Ndafowoka ndikupempha chithandizo; kummero kwanga kwawuma gwaa, mʼmaso mwanga mwada kuyembekezera Mulungu wanga.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

3 Ndalema ndi kufuula kwanga; kum'mero kwauma gwaa! M'maso mwanga mwada poyembekeza Mulungu wanga.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Ndalema ndi kufuula kwanga; kum'mero kwauma gwa! M'maso mwanga mwada poyembekeza Mulungu wanga.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Ndafooka ndi kulira kwanga, kum'mero kwanga kwauma. M'maso mwada pamene ndikuyembekezera Mulungu wanga.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 69:3
18 Mawu Ofanana  

Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”


Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;


Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.


Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”


Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.


Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.


Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.


“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani? Chiyembekezo changa chili mwa Inu.


Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga, nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga. Ambiri adzaona, nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.


Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.


Iwo anayika ndulu mʼchakudya changa ndi kundipatsa vinyo wosasa chifukwa cha ludzu.


Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. Sela


Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba, ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula. Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga. Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”


Maso anga atopa ndi kulira, ndazunzika mʼmoyo mwanga, mtima wanga wadzaza ndi chisoni chifukwa anthu anga akuwonongeka, chifukwa ana ndi makanda akukomoka mʼmisewu ya mu mzinda.


Atadziwa kuti zonse zatha tsopano komanso kuti malemba akwaniritsidwe, Yesu anati, “Ine ndili ndi ludzu.”


Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.


Yesu, pa nthawi imene anali munthu pa dziko lapansi pano, anapereka mapemphero ake ndi zopempha mofuwula ndi misozi kwa Iye amene akanamupulumutsa ku imfa, ndipo anamumvera chifukwa anagonjera modzipereka.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa