Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 2:2 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

2 Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi, nachita upo akulu pamodzi, Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wake, ndi kuti,

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

2 Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi, nachita upo akulu pamodzi, Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wake, ndi kuti,

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

2 Mafumu ao akuchita upo, olamula ao akhala pamodzi kuti apangane zoipa, zoukira Chauta ndi mfumu yake yodzozedwa.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 2:2
27 Mawu Ofanana  

Ambuye ali kudzanja lako lamanja; Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake.


Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.


Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.


Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,


iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.


Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.


Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.


Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,


Ndamupeza mtumiki wanga Davide; ndamudzoza ndi mafuta opatulika.


Ndipo mmawa mudzaona ulemerero wa Yehova pakuti wamva kudandaula kwanu. Kodi ife ndi yani kuti muzitidandaulira?”


Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.


Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine, chifukwa Yehova wandidzoza kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka. Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima, ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.


Herode atazindikira kuti Anzeruwo anamupusitsa, anakwiya kwambiri. Ndipo anatumiza anthu kukapha ana onse aamuna a mʼBetelehemu ndi midzi yozungulira amene anali a zaka ziwiri kapena zocheperapo, molingana ndi nthawi imene Anzeruwo anamuwuza.


Pamenepo akulu a ansembe ndi akuluakulu anasonkhana ku nyumba ya mkulu wa ansembe dzina lake Kayafa,


Akulu a ansembe ndi akulu olamulira Ayuda amafunafuna umboni wonama wofuna kuphera Yesu.


Mmamawa, akulu a ansembe onse ndi akuluakulu anavomerezana kuti aphe Yesu.


Pa nthawi imeneyo Afarisi anabwera kwa Yesu ndipo anati kwa Iye, “Chokani malo ano ndipo pitani kumalo ena aliwonse. Herode akufuna kukuphani.”


Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).


Iye amene amadana ndi Ine amadananso Atate anga.


Pakuti amene Mulungu wamutuma amayankhula mawu a Mulungu; Mulungu wamupatsa Mzimu Woyera mopanda malire.


kuti Mulungu, anamudzoza Yesu, wa ku Nazareti ndi Mzimu Woyera ndi mphamvu ndiponso mmene Iye anapita nachita zabwino ndi kuchiritsa onse amene anali pansi pa mphamvu ya mdierekezi, popeza kuti Mulungu anali naye.


Iye anagwa pansi ndipo anamva mawu akuti, “Saulo, Saulo ukundizunziranji Ine?”


Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa