Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Genesis 4:6 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa?

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

6 Ndipo Yehova anati kwa Kaini, Ukwiyiranji? Yagweranji nkhope yako?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Ndipo Yehova anati kwa Kaini, Ukwiyiranji? Yagweranji nkhope yako?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Apo Chauta adafunsa Kainiyo kuti, “Kodi wakwiyiranji chotere? Chifukwa chiyani nkhope yako yagwa?

Onani mutuwo Koperani




Genesis 4:6
13 Mawu Ofanana  

Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”


Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.


Yehova akuti, “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu. Ngakhale machimo anu ali ofiira, adzayera ngati thonje. Ngakhale ali ofiira ngati kapezi, adzayera ngati ubweya wankhosa.


“Inu anthu a mʼbado uno, ganizirani bwino mawu a Yehova: “Kodi Ine ndinakhalapo ngati chipululu kwa Israeli kapena ngati dziko la mdima wandiweyani? Chifukwa chiyani anthu anga akunena kuti, ‘Ife tili ndi ufulu omayendayenda; sitidzabweranso kwa Inu’?


Yehova akuti, “Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji, kuti andithawe? Iwo anatsata milungu yachabechabe, nawonso nʼkusanduka achabechabe.


Koma Yehova anayankha kuti, “Kodi nʼkoyenera kuti iwe ukwiye?”


Koma Mulungu anati kwa Yona, “Kodi nʼkoyenera kuti iwe ukwiye chifukwa cha msatsi?” Iye anayankha kuti, “Inde nʼkoyenera. Kukwiya kwanga nʼkofuna kufa nako.”


Kodi ndilibe ufulu wochita zimene ndikufuna ndi ndalama zanga? Kapena ukuyipidwa chifukwa ndine wopereka mowolowamanja?’


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa