Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Genesis 10:4 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

4 Ndi ana aamuna a Yavani: Elisa, ndi Tarisisi, ndi Kitimu, ndi Dodanimu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Ndi ana amuna a Yavani: Elisa, ndi Tarisisi, ndi Kitimu, ndi Dodanimu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 Ana a Yavani anali Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Dodanimu.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 10:4
10 Mawu Ofanana  

(Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).


Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.


Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.


Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”


“Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.


“Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali zonyamula malonda ako. Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi yodzaza ndi katundu wolemera.


Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani anapanga zopalasira zako; ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu. Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.


Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako, ndipo inakhala ngati mbendera. Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo zochokera ku zilumba za Elisa.


Sitima zapamadzi zochokera ku mayiko a ku madzulo zidzalimbana naye, ndipo adzataya mtima. Kenaka idzabwerera mopsa mtima ndi kudzalimbana ndi chipembedzo cha anthu opatulika. Idzabwerera ndi kuchitira chifundo amene sadzasunga pangano loyera.


Sitima zapamadzi zidzabwera kuchokera ku madooko a Kitimu; kupondereza Asuri ndi Eberi, koma iwonso adzawonongeka.”


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa