Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Filemoni 1:13 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

13 Ndikanakonda ndikanakhala naye kuno kuti iyeyo azinditumikira mʼmalo mwako pamene ndili mu unyolo chifukwa cha Uthenga Wabwino.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

13 Ameneyo ndikadafuna ine kumsunga akhale nane, kuti m'malo mwako akadanditumikira ine m'ndende za Uthenga Wabwino:

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

13 Ameneyo ndikadafuna ine kumsunga akhale nane, kuti m'malo mwako akadanditumikira ine m'ndende za Uthenga Wabwino:

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

13 Ndikadakonda kuti akhalebe ndi ine kuno, kuti azinditumikira m'malo mwako, pokhala ndili m'ndende chifukwa cha Uthenga Wabwino.

Onani mutuwo Koperani




Filemoni 1:13
8 Mawu Ofanana  

Ndikondwera kuti Stefano, Fortunato ndi Akayiko afika, chifukwa akhala akundithandiza pakuti inu simuli nane.


Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.


Ine monga wamʼndende chifukwa chotumikira Ambuye, ndikukulimbikitsani kuti mukhale moyo woyenera mayitanidwe amene munalandira.


Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu.


Iyeyu anatsala pangʼono kufa chifukwa cha ntchito ya Khristu, anayika moyo pa chiswe kuti akwaniritse thandizo limene inu simukanatha.


Kuchokera kwa Paulo, amene ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu ndi Timoteyo mʼbale wathu. Kulembera Filemoni, bwenzi lathu lokondedwa ndi mtumiki mnzathu.


ndikukupempha chifukwa cha mwana wanga Onesimo, amene ndamubala ndili mu unyolo.


Ine ndikumutumizanso kwa iwe tsopano, koma potero ndikukhala ngati ndikutumiza mtima wanga weniweni.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa