Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Eksodo 9:21 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

21 Koma iwo amene ananyozera mawu a Yehova anasiya akapolo ndi ziweto zawo panja.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

21 koma iyeyu wosasamalira mau a Yehova anasiya anyamata ndi zoweta zake kubusa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

21 koma iyeyu wosasamalira mau a Yehova anasiya anyamata ndi zoweta zake kubusa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

21 Komabe ena sadasamaleko zimene Chauta adanenazo, ndipo adangosiya panja akapolo ao pamodzi ndi zoŵeta zomwe.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 9:21
11 Mawu Ofanana  

Tsono perekani mtima wanu ndi moyo wanu kufunafuna Yehova Mulungu wanu. Yambani kumanga malo opatulika a Yehova Mulungu, kuti mubweretse Bokosi la Chipangano la Yehova ndi zinthu zopatulika za Mulungu mʼNyumba ya Mulungu imene idzamangidwa chifukwa cha dzina la Yehova.”


Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,


“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,


Mʼmalo mwake iye anatembenuka ndi kupita ku nyumba yake yaufumu ndipo zimenezi sanazilabadire.


Nduna za Farao zinachita mantha ndi mawu a Yehova, ndipo zinalowetsa antchito awo ndi ziweto zawo mʼnyumba.


Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kweza dzanja lako kumwamba kuti matalala agwe pa dziko lonse la Igupto, pa munthu aliyense, pa ziweto ndi pa zonse zomera mʼminda ya Igupto.”


Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.


Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:


Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”


Ndipo iye anapitiriza nati, “Usachite mantha Danieli. Kuyambira tsiku loyamba pamene unatsimikiza mtima kuti umvetse zinthuzi ndi kudzichepetsa pamaso pa Mulungu wako, pempho lako linamveka ndipo ndabwera kudzayankha mapemphero akowo.


Popeza mkaziyo anali pafupi kumwalira, akazi amene amamuthandiza anati, “Usaope, wabereka mwana wamwamuna” Koma iye sanayankhe kapena kulabadirako.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa