Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Eksodo 8:12 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

12 Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

12 Ndipo Mose ndi Aroni anatuluka kwa Farao; ndi Mose anafuulira kwa Yehova kunena za achule amene adawaika pa Farao.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

12 Ndipo Mose ndi Aroni anatuluka kwa Farao; ndi Mose anafuulira kwa Yehova kunena za achule amene adawaika pa Farao.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

12 Pamenepo Mose ndi Aroni adachoka kwa Farao kuja, ndipo adakapempha Chauta kuti achotse achule amene adaatumiza kwa Farao aja.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 8:12
10 Mawu Ofanana  

Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.


Mose anachoka kwa Farao nakapemphera kwa Yehova.


Koma Mose anapempha chifundo cha Mulungu wake ndipo anati, “Chonde Yehova, chifukwa chiyani mwakwiyira anthu awa amene munawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.


Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa


Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova.


Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”


Mose anasiyana ndi Farao natuluka mu mzindawo. Iye anakweza manja ake kwa Yehova. Mabingu ndi matalala zinaleka, ndipo mvula inalekeratu kugwa mʼdzikolo.


“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzalolanso Aisraeli kuti andipemphe zoti ndiwachitire: Ndidzachulukitsa anthu awo ngati nkhosa.


Ndiponso kunena za ine, zisachitike kuti ndichimwire Yehova pakulephera kukupemphererani. Ndipo ine ndidzakuphunzitsani njira yabwino ndi yolungama kuti muziyendamo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa