Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Eksodo 6:9 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

9 Mose anawafotokozera Aisraeli zimenezi, koma iwo sanamumvere chifukwa cha kukhumudwa ndi goli lankhanza.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

9 Ndipo Mose ananena chomwecho ndi ana a Israele; koma sanamvere Mose chifukwa cha kuwawa mtima, ndi ukapolo wolemera.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

9 Ndipo Mose ananena chomwecho ndi ana a Israele; koma sanamvere Mose chifukwa cha kuwawa mtima, ndi ukapolo wolemera.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

9 Mose adauza Aisraele zimenezi, koma iwo sadamvere, chifukwa choti anali atataya kale mtima, pomakhala mu ukapolo wao mwankhalwe chotere.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 6:9
9 Mawu Ofanana  

“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?


Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.


Kodi sindizo zimene tinakuwuza mʼdziko la Igupto? Ife tinati, ‘Tileke titumikire Aigupto?’ Zikanatikomera kutumikira Aigupto kulekana ndi kufa mʼchipululu muno.”


Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu.


ndipo iwo anati, “Yehova akupenyeni ndi kukuweruzani popeza mwachititsa Farao ndi nduna zake kuti anyansidwe nafe ndipo mwayika lupanga mʼmanja mwawo kuti atiphe.”


Kenaka Yehova anati kwa Mose,


Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.


Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.


Aisraeli anayenda kuchokera ku phiri la Hori kudzera njira ya ku Nyanja Yofiira kuzungulira dziko la Edomu. Koma anthu anataya mtima mʼnjiramo


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa