Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Eksodo 5:12 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

12 Kotero anthuwo anamwazikana mʼdziko lonse la Igupto kukamweta udzu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

12 Pamenepo anthuwo anabalalika m'dziko lonse la Ejipito kufuna chiputu ngati udzu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

12 Pamenepo anthuwo anabalalika m'dziko lonse la Ejipito kufuna chiputu ngati udzu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

12 Motero anthu aja adamwazikira m'dziko lonse la Ejipito kukafunafuna udzuwo.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 5:12
9 Mawu Ofanana  

Ndi ulemerero wanu waukulu, munagonjetsa okutsutsani. Inu munatumiza mkwiyo wanu waukulu; ndipo unawapsereza ngati udzu.


Mʼmalo mwake mupite mukadzimwetere udzu kulikonse kumene mungawupeze. Komabe ntchito yanu sichepetsedwa.’ ”


Akapitawo a thangata aja anawafulumiza anthu aja nati, “Malizani kugwira ntchito yanu ya tsiku ndi tsiku monga mmene zinalili pamene munkapatsidwa udzu.”


Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi; adzapsa ndi moto. Sangathe kudzipulumutsa okha ku mphamvu ya malawi a moto. Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha; kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.


Nʼchifukwa chake monga momwe moto umawonongera chiputu ndipo monga momwe udzu wowuma umapsera mʼmalawi a moto, momwemonso mizu yawo idzawola ndipo maluwa awo adzafota ndi kuwuluka ngati fumbi; chifukwa akana malamulo a Yehova Wamphamvuzonse, ndipo anyoza mawu a Woyerayo wa Israeli.


Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.


Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto; nyumba ya Esau idzasanduka chiputu, ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza. Sipadzakhala anthu opulumuka kuchokera mʼnyumba ya Esau.” Yehova wayankhula.


Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.


Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa