Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Eksodo 40:7 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

7 Uyike beseni pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo uyikemo madzi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

7 Ukaikenso mkhate pakati pa chihema chokomanako, ndi guwa la nsembe, ndi kuthiramo madzi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

7 Ukaikenso mkhate pakati pa chihema chokomanako, ndi guwa la nsembe, ndi kuthiramo madzi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

7 Beseni uliike pakati pa chihema chamsonkhano ndi guwa, ndipo uthiremo madzi.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 40:7
11 Mawu Ofanana  

Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,


Anapanga beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso kuchokera ku magalasi oyangʼanira nkhope a amayi amene ankatumikira pa chipata cha tenti ya msonkhano.


“Uyike guwa lansembe yopsereza patsogolo pa chipata cha chihema, tenti ya msonkhano.


Upange bwalo lozungulira chihemacho ndipo uyike katani ya pa chipata cha bwalolo.


“Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.


Iye anatipulumutsa, osati chifukwa cha ntchito zathu zolungama zimene tinachita koma chifukwa cha chifundo chake. Anatipulumutsa potisambitsa, kutibadwitsa kwatsopano ndi kutikonzanso mwa Mzimu Woyera


Tsono tiyeni tiyandikire kwa Mulungu ndi mtima woona ndi wodzaza ndi chikhulupiriro. Popeza mitima yathu yayeretsedwa, ndi yopanda chikumbumtima chotitsutsa, ndiponso matupi athu asambitsidwa ndi madzi woyera.


Koma tikamayenda mʼkuwunika, monga Iye ali mʼkuwunika, pamenepo timayanjana wina ndi mnzake, ndipo magazi a Yesu, Mwana wake, amatitsuka ndi kutichotsera tchimo lililonse.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa