Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Eksodo 22:6 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 “Ngati munthu ayatsa moto, motowo ndikukafika mpaka ku munda ndi kuwotcha mulu wa tirigu kapena tirigu wosadula, kapena munda wonse, ndiye kuti munthu amene anayatsa motoyo alipire.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

6 Ukayaka moto, nukalandira kuminga, kotero kuti unyeketsa mulu wa tirigu, kapena tirigu wosasenga, kapena munda; woyatsa motoyo alipe ndithu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Ukayaka moto, nukalandira kuminga, kotero kuti unyeketsa mulu wa tirigu, kapena tirigu wosasenga, kapena munda; woyatsa motoyo alipe ndithu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 “Moto ukabuka mpaka kukafika ku thengo, ndipo ukatentha mulu wa tirigu kapena tirigu wosadula kapena munda umene uli ndi mbeu, amene adatenthayo alipire zoonongekazo.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 22:6
8 Mawu Ofanana  

Koma ngati chiwetocho chinabedwa, iye ayenera kubwezera mwini wakeyo.


“Ngati munthu alekerera ziweto zake kukalowa mʼmunda wa munthu wina kukadya mbewu zake, munthuyo amubwezere mwini mundawo mbewu zina zabwino kapena mpesa wina wabwino kwambiri.


“Ngati munthu asungitsidwa ndi mnzake ndalama kapena katundu, ndipo zinthu zija nʼkubedwa mʼnyumba mwake, wakubayo ngati agwidwa, ayenera kubwezera kawiri chobedwacho.


Ngati pali kukangana kokhudza ngʼombe, bulu, nkhosa, zovala kapena kanthu kalikonse kotayika, ndipo mmodzi ndikunena kuti chinthucho nʼchake, awiriwo abwere nawo mlandu wawowo pamaso pa Mulungu ndipo amene mlandu umugomere adzayenera kumulipira mnzakeyo kawiri.


Mudzawazindikira iwo ndi zipatso zawo. Kodi anthu amathyola mpesa pa mtengo wa minga, kapena nkhuyu pa nthula?


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa