Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Eksodo 20:9 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

9 Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

9 Masiku asanu ndi limodzi uzigwira, ndi kumaliza ntchito zako zonse;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

9 Masiku asanu ndi limodzi uzigwira, ndi kumaliza ntchito zako zonse;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

9 Masiku asanu ndi limodzi uzigwira ntchito zako zonse.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 20:9
10 Mawu Ofanana  

Muzitola chakudya masiku asanu ndi limodzi koma tsiku la chisanu ndi chiwiri ndi la Sabata, simukapeza chilichonse kunjaku.”


“Muzigwira ntchito masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri musagwire ntchito kuti ngʼombe yanu ndi bulu wanu apume ndiponso kuti kapolo wobadwira mʼnyumba yanu ndi mlendo yemwe apezenso mphamvu.


Mugwire ntchito kwa masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, lopuma, tsiku lopatulika la Yehova. Aliyense amene agwira ntchito iliyonse pa tsiku la Sabata ayenera kuphedwa.


“Muzigwira ntchito masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri, musagwire ntchito ina iliyonse, Ngakhale nthawi yolima ndi yokolola muyenera kupuma.


Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.


Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”


“Ambuye Yehova akuti, Chipata chakummawa cha bwalo lamʼkati chizikhala chotseka pa masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito, koma chizitsekulidwa pa tsiku la sabata ndi pa tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano.


“ ‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.


Chifukwa cha kuyipidwa kuti Yesu anachiritsa pa Sabata, wolamulira sunagoge anati kwa anthu, “Pali masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito. Choncho bwerani kuti mudzachiritsidwe masiku amenewo osati pa Sabata.”


Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa