Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Eksodo 17:8 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

8 Amaleki anabwera ku Refidimu kudzamenyana ndi Aisraeli.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

8 Pamenepo anadza Amaleke, nayambana ndi Israele mu Refidimu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

8 Pamenepo anadza Amaleke, nayambana ndi Israele m'Refidimu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

8 Tsono kudabwera Aamaleke ku Refidimu kudzamenyana ndi Aisraele.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 17:8
13 Mawu Ofanana  

Kenaka anabwerera napita ku Eni-Misipati (ku Kadesi), ndipo anagonjetsa dera lonse la Aamaleki, kuphatikizanso Aamori amene ankakhala ku Hazazoni Tamara.


Timna anali mzikazi wa Elifazi, mwana wa Esau. Iyeyo anaberekera Elifazi mwana dzina lake Amaleki. Amenewa ndiwo zidzukulu za Ada, mkazi wa Esau.


Kora, Gatamu, ndi Amaleki. Awa anali mafumu mwa ana a Elifazi ku Edomu ndipo onsewa anali zidzukulu za Ada.


Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.


Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku chipululu cha Sini, ndi kumayenda malo ndi malo monga momwe anawalamulira Yehova. Iwo anamanga misasa yawo ku Refidimu koma kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa.


Aamaleki amakhala ku Negevi, Ahiti, Ayebusi ndi Aamori amakhala mʼdziko la mapiri ndipo Akanaani amakhala pafupi ndi nyanja, mʼmbali mwa Yorodani.”


Kenaka Balaamu anaona Aamaleki ndipo ananena uthenga wake uwu: “Aamaleki anali oyamba mwa mitundu ya anthu koma potsiriza pake adzawonongeka.”


Aisraeli amati akadzala mbewu, Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena akummawa amabwera ndi kudzawathira nkhondo.


Anachita nkhondo mwamphamvu ndi kugonjetsa Aamaleki. Choncho anapulumutsa Aisraeli mʼmanja mwa anthu amene ankawalanda zinthu zawo.


Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzalanga Aamaleki chifukwa cha zimene anawachita Aisraeli. Paja iwo analimbana ndi Aisraeli pa njira pamene Aisraeliwo ankachoka ku Igupto.


Tsono Davide ndi anthu ake ankapita kukathira nkhondo Agesuri, Agirizi ndi Aamaleki. (Mitundu ya anthu imeneyi kuyambira kale inkakhala mʼdziko la pakati pa Suri ndi Igupto).


Pa tsiku lachitatu, Davide ndi anthu ake anakafika ku Zikilagi. Tsono anapeza Aamaleki atawononga kale dera la Negevi ndi Zikilagi. Anathira nkhondo mzinda wa Zikilagi ndi kuwutentha ndi moto.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa