Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Eksodo 15:5 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Nyanja yakuya inawaphimba; Iwo anamira pansi ngati mwala.”

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

5 Nyanja inawamiza; anamira mozama ngati mwala.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Nyanja inawamiza; anamira mozama ngati mwala.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Nyanja yozamayo idaŵaphimba onse, adamira mpaka pansi pa nyanja ngati miyala.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 15:5
12 Mawu Ofanana  

Inu munagawa nyanja anthu anu akupenya, kotero kuti anadutsa powuma, koma munamiza mʼmadzi akuya anthu amene ankawalondola monga mmene uchitira mwala mʼmadzi ozama.


Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.


Madzi anabwerera ndi kumiza magaleta ndi okwera akavalo, asilikali ankhondo onse amene anatsatira Aisraeli mʼnyanja, palibe ndi mmodzi yemwe amene anapulumuka.


Koma Inu munawuzira mphepo yanu, ndipo nyanja inawaphimba. Iwo anamira ngati chitsulo mʼmadzi amphamvu.


Onse agwidwa ndi mantha woopsa. Popeza anaona mphamvu zanu zazikulu, iwo ayima chilili ngati mwala mpaka anthu anu, Inu Yehova atadutsa; inde mpaka atadutsa anthu amene munawagula.


Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.


Koma tsopano wathyokera mʼnyanja, pansi penipeni pa nyanja. Katundu wako ndi onse amene anali nawe amira pamodzi nawe.


Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga.


Inu mudzatichitiranso chifundo; mudzapondereza pansi machimo athu ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.


“Koma ngati wina aliyense achimwitsa mmodzi wa ana awa, amene akhulupirira Ine, kuti achimwe, kukanakhala bwino kuti iye amangiriridwe chimwala chachikulu mʼkhosi mwake ndi kumizidwa pansi pa nyanja.


Kenaka mngelo wamphamvu ananyamula mwala waukulu ngati mphero yayikulu nawuponya mʼnyanja nanena kuti, “Mwa mphamvu chonchi mzinda waukulu wa Babuloni udzaponyedwa pansi, sudzapezekanso.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa