Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Eksodo 13:10 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Muzichita mwambo uwu pa nthawi yake chaka ndi chaka.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

10 Chifukwa chake uzikasunga lemba ili pa nyengo yake chaka ndi chaka.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Chifukwa chake uzikasunga lemba ili pa nyengo yake chaka ndi chaka.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Musunge malangizo ameneŵa pa nthaŵi yake chaka ndi chaka.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 13:10
8 Mawu Ofanana  

“Ili ndi tsiku la chikumbutso. Tsiku limeneli muzidzachita chikondwerero, kupembedza Yehova. Mibado yonse imene ikubwera izidzakumbukira tsiku limeneli ngati lamulo lamuyaya ndi kuti pa tsikuli azidzachita chikondwerero cholemekeza Yehova.


“Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti, chifukwa ndi pa tsiku limeneli ndinatulutsa magulu anu mʼdziko la Igupto. Muzikondwerera tsiku limeneli pa mibado yonse ngati lamulo lamuyaya.


Usiku wonse Yehova anachezera kutulutsa ana a Israeli mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake pa tsiku limeneli Aisraeli onse azichezera usiku wonse kulemekeza Mulungu kamba ka mibado yonse ya mʼtsogolo.


Yehova akadzakulowetsani mʼdziko la Akanaani, Ahiti, Aamori, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi, muzikachita mwambo uwu mwezi uno.


“Muzichita Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti monga ndinakulamulirani. Muzichita zimenezi mwezi wa Abibu pa nthawi yomwe ndayika, pakuti mʼmwezi umenewu munatuluka mʼdziko la Igupto. “Pasapezeke munthu wobwera pamaso panga wopanda kanthu mʼmanja.


Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa