Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 12:2 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 “Mwezi uno uzikhala mwezi wanu woyamba wa chaka.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

2 Mwezi uno uzikhala kwa inu woyamba wa miyezi; muziuyesa mwezi woyamba wa chaka.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

2 Mwezi uno uzikhala kwa inu woyamba wa miyezi; muziuyesa mwezi woyamba wa chaka.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

2 “Mwezi uno udzakhala mwezi wanu woyambira chaka.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 12:2
14 Mawu Ofanana  

Mwezi woyamba, umene ndi mwezi wa Nisani, chaka cha khumi ndi chiwiri cha ufumu wa Ahasiwero anachita maere, otchedwa Purimu pamaso pa Hamani kuti apeze tsiku ndi mwezi woyenera. Ndipo maere anagwera pa mwezi wa khumi ndi chiwiri ndiwo mwezi wa Adara.


Yehova anayankhula kwa Mose ndi Aaroni mʼdziko la Igupto kuti,


Mwezi woyamba muzidzadya buledi wopanda yisiti kuyambira madzulo tsiku la 14 la mweziwo mpaka tsiku la 21 mwezi womwewo.


Muliwuze khamu lonse la Israeli kuti pa tsiku la khumi la mwezi uno, munthu aliyense asankhire banja lake mwana wankhosa mmodzi. Banja lililonse litenge mwana wankhosa mmodzi.


Ndipo Mose anati kwa anthu, “Muzikumbukira tsiku lino, tsiku limene munatuluka mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo chifukwa Yehova anakutulutsani ndi dzanja lake lamphamvu. Musadye kalikonse kamene kali ndi yisiti.


Pa tsiku la lero mwezi uno wa Abibu, mukutuluka mʼdziko la Igupto.


“Muzichita Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti monga ndinakulamulirani. Muzichita zimenezi mwezi wa Abibu pa nthawi yomwe ndayika, pakuti mʼmwezi umenewu munatuluka mʼdziko la Igupto. “Pasapezeke munthu wobwera pamaso panga wopanda kanthu mʼmanja.


“Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti. Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti monga momwe ndinakulamulirani. Muzichita zimenezi pa nthawi yoyikika mwezi wa Abibu, pakuti mwezi umenewu inu munatuluka mʼdziko la Igupto.


Kotero anayimika chihema tsiku loyamba la mwezi woyamba mʼchaka chachiwiri.


“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.


“ ‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.


Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.


“ ‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.


Samalirani mwezi wa Abibu ndi kukondwerera Paska wa Yehova Mulungu wanu, chifukwa pa mwezi wa Abibu, usiku, Iye anakutulutsani mu Igupto.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa