Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Eksodo 10:10 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Farao anati, “Yehova akhale ndi inu ngati ndingakuloleni kupita pamodzi ndi akazi ndi ana anu! Zikuoneka kuti mwakonzeka kuchita choyipa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

10 Ndipo ananena nao, Momwemo, Yehova akhale nanu ngati ndilola inu ndi ana aang'ono anu mumuke; chenjerani pakuti pali choipa pamaso panu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Ndipo ananena nao, Momwemo, Yehova akhale nanu ngati ndilola inu ndi ana ang'ono anu mumuke; chenjerani pakuti pali choipa pamaso panu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Choncho Farao adaŵauza kuti, “Chauta akhale nanu ngati ine ndikulolani kuti mutenge akazi anu ndi ana anu. Nchodziŵikiratu kuti inu mukufuna kudzetsa mavuto.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 10:10
7 Mawu Ofanana  

Choncho inu musalole kuti Hezekiya akunamizeni ndi kukusocheretsani motere. Musamukhulupirire, pakuti palibe mulungu wa mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse umene unatha kupulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa kapena mʼdzanja la makolo anga. Nanga bwanji Mulungu wanuyo, sadzatha kukupulumutsani kuchoka mʼdzanja langa!”


Ndakana! Amuna okha ndiwo apite ndi kukapembedza Yehova pakuti izi ndi zimene mwakhala mukupempha.” Kenaka Mose ndi Aaroni anathamangitsidwa pamaso pa Farao.


Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kapembedzeni Yehova. Ngakhale akazi ndi ana anu apite pamodzi ndi inu. Koma musatenge ziweto zanu ndi ngʼombe zanu.”


Mose anayankha kuti, “Ife tidzapita tonse pamodzi; angʼonoangʼono ndi akuluakulu, ana athu aamuna ndi aakazi, ndiponso ziweto zathu ndi ngʼombe chifukwa tikakhala ndi chikondwerero cha kwa Yehova.”


Nthawi yamasana Yehova amakhala patsogolo pa anthu kuwatsogolera njira ndi chipilala cha mtambo, ndipo usiku Yehova ankawatsogolera ndi chipilala cha moto, kuwawunikira njira kuti athe kuyenda masana ndi usiku.


Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa