Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Danieli 5:30 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

30 Usiku womwewo Belisazara, mfumu ya anthu a ku Babuloni, inaphedwa,

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

30 Usiku womwewo Belisazara mfumu ya Ababiloni anaphedwa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

30 Usiku womwewo Belisazara mfumu ya Ababiloni anaphedwa.

Onani mutuwo Koperani




Danieli 5:30
9 Mawu Ofanana  

Koma mʼkamphindi, ndiponso tsiku limodzi, zinthu ziwiri izi zidzakuchitikira: ana ako kukufera komanso kukhala mkazi wamasiye. Zimenezi zidzakuchitikira kwathunthu ngakhale ali ndi amatsenga ambiri ndi mawula amphamvu.


Ndinakutchera msampha, iwe Babuloni, ndipo wakodwamo iwe wosazindikira kanthu; unapezeka ndiponso unakodwa chifukwa unalimbana ndi Yehova.


“Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi, popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni. Motero adzalipsira Ababuloni chifukwa chowononga Nyumba yake. Ndiye Yehova akuti, ‘Nolani mivi, tengani zishango.’


Othamanga akungopezanapezana, amithenga akungotsatanatsatana kudzawuza mfumu ya ku Babuloni kuti alande mzinda wake wonse.


Ngati achita dyera ndiye ndidzawakonzera madyerero ndi kuwaledzeretsa, kotero kuti adzasangalala, kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,” akutero Yehova.


Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake, abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo; adzagona kwamuyaya osadzukanso,” akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.


Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo; maphwando ndi zikondwerero zanu zidzatheratu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa