Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Danieli 10:18 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

18 Kenaka wooneka ngati munthu uja anandikhudzanso ndipo anandipatsa mphamvu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

18 Pamenepo anandikhudzanso wina, maonekedwe ake ngati munthu, nandilimbikitsa ine.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

18 Pamenepo anandikhudzanso wina, maonekedwe ake ngati munthu, nandilimbikitsa ine.

Onani mutuwo Koperani




Danieli 10:18
16 Mawu Ofanana  

Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.


Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.


Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.


Dzanja linandikhudza ndi kundinyamula ndipo ndinachita ngati kuwerama pa mawondo manja atagwira pansi.


Kenaka wina wa maonekedwe ngati munthu anakhudza milomo yanga, ndipo ndinatsekula pakamwa panga ndi kuyamba kuyankhula. Ndinati kwa amene anayima patsogolo panga, “Ine ndasweka mtima chifukwa cha masomphenyawa mbuye wanga, ndipo ndalefuka.


Ine Danieli ndikuyangʼanitsitsa masomphenyawa ndi kuyesa kuwazindikira, kuwamvetsa, ndinangoona wina wooneka ngati munthu atayima patsogolo panga.


Pamene ankandiyankhula ndinadzigwetsa pansi chafufumimba, nʼkugona tulo tofa nato. Kenaka anandikhudza ndi kundiyimiritsa.


Koma Ine ndakupempherera Simoni, kuti chikhulupiriro chako chisafowoke ndipo pamene udzabwerera kwa Ine, udzalimbikitse abale ako.”


Mngelo wochokera kumwamba anafika namulimbikitsa.


Atakhala kwa kanthawi ku Antiokeya, Paulo anachokako nayendera madera onse a ku Galatiya ndi ku Frugiya kulimbikitsa ophunzira onse.


Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake,


Ndikhoza kuchita zonse kudzera mwa Iye amene amandipatsa mphamvu.


Timapempheranso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu yake yonse ya ulemerero wake, kuti muzipirira zonse ndi mitima yofatsa ndi ya chimwemwe


Davide anaona kuti Sauli akufunafuna kuti amuphe. Nthawiyi nʼkuti Davide ali mʼchipululu cha Zifi ku Horesi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa