Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Afilipi 4:4 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Nthawi zonse muzikondwa mwa Ambuye. Ndikubwerezanso; muzikondwa!

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

4 Kondwerani mwa Ambuye nthawi zonse: ndibwerezanso kutero, kondwerani.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Kondwerani mwa Ambuye nthawi zonse: ndibwerezanso kutero, kondwerani.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 Muzikondwa mwa Ambuye nthaŵi zonse. Ndikubwerezanso kuti, “Muzikondwa.”

Onani mutuwo Koperani




Afilipi 4:4
18 Mawu Ofanana  

Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.


Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.


komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.


Sangalalani, kondwerani chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba, chifukwa moterenso ndi mmene anazunzira aneneri inu musanabadwe.


Koma pakati pa usiku Paulo ndi Sila ankapemphera ndi kuyimba nyimbo zolemekeza Mulungu, ndipo akayidi ena ankamvetsera.


Iwo anachoka ku Bwalo Lalikulu akukondwa chifukwa anayesedwa oyenera kunyozedwa chifukwa cha dzina la Yesu.


Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero.


Amatiyesa achisoni, koma ndife achimwemwe nthawi zonse, aumphawi, koma olemeretsa ambiri; wopanda kanthu, koma tili ndi zonse.


Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa!


Chomwechonso, inu khalani okondwa ndi osangalala nane pamodzi.


Abale anga, ndikupitiriza kunena kuti, kondwani mwa Ambuye! Sizondivuta kuti ndilembenso mawu omwewo, ndipo zimenezi nʼzokuthandizani inuyo.


Koma kondwerani popeza mukumva zowawa pamodzi ndi Khristu, kuti mudzakondwere kwakukulu pamene ulemerero wake udzaonekera.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa