Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Afilipi 3:7 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

7 Koma zonse zimene ndinkaziyesa zaphindu, tsopano ndikuziona kuti nʼzosapindulitsa chifukwa cha Khristu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

7 Komatu zonse zimene zinandipindulira, zomwezo ndinaziyesa chitayiko chifukwa cha Khristu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

7 Komatu zonse zimene zinandipindulira, zomwezo ndinaziyesa chitayiko chifukwa cha Khristu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

7 Koma chifukwa cha Khristu, zomwe kale ndinkaziyesa zaphindu, tsopano ndikuziwona kuti nzosapindula.

Onani mutuwo Koperani




Afilipi 3:7
20 Mawu Ofanana  

Atangowatulutsa, mmodzi wa angelowo anati, “Thawani kuti mudzipulumutse, musachewuke, musayime pena paliponse mʼchigwamo! Thawirani ku mapiri kuopa kuti mungawonongeke!”


Koma mkazi wa Loti anachewuka ndipo anasanduka mwala wa mchere.


Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo.


Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.


Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.


Nthawi yofunafuna ndi nthawi yoleka kufunafuna, nthawi yosunga ndi nthawi yotaya.


Kodi munthu adzapindula chiyani ngati atapeza zonse za dziko lapansi nataya moyo wake? Kapena munthu angapereke chiyani chosinthana ndi moyo wake?


Anaponya mkanjo wake kumbali, analumpha nabwera kwa Yesu.


“Ngati wina aliyense abwera kwa Ine ndipo sadana ndi abambo ndi amayi ake, mkazi wake ndi ana, abale ake ndi alongo ake, inde ngakhale moyo wake omwe, iye sangakhale ophunzira wanga.


Mʼnjira yomweyo, wina aliyense wa inu amene sasiya zonse ali nazo sangakhale ophunzira wanga.


“Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika.


Onse atadya, nakhuta anapeputsa sitimayo potaya tirigu mʼnyanja.


Anaona kuti kuzunzika chifukwa cha Khristu kunali kwa mtengowapatali kuposa chuma cha ku Igupto, chifukwa amaona mphotho ya mʼtsogolo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa