Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Afilipi 2:4 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Musamangofuna zokomera inu nokha koma aliyense azifuna zokomeranso ena.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

4 munthu yense asapenyerere zake za iye yekha, koma yense apenyererenso za mnzake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 munthu yense asapenyerere zake za iye yekha, koma yense apenyererenso za mnzake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 Musamangofuna zokomera inu nokha, koma zokomeranso anzanu.

Onani mutuwo Koperani




Afilipi 2:4
15 Mawu Ofanana  

Koma Mordekai atazindikira za chiwembuchi anawuza mfumukazi Estere ndipo iye anakawuza mfumu mʼmalo mwa Mordekai.


Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno?


“Koma ngati wina aliyense achimwitsa mmodzi wa ana awa, amene akhulupirira Ine, kuti achimwe, kukanakhala bwino kuti iye amangiriridwe chimwala chachikulu mʼkhosi mwake ndi kumizidwa pansi pa nyanja.


Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira.


Ife amene tili ndi chikhulupiriro champhamvu tiziwalezera mtima anthu ofowoka, ndipo tisamadzikondweretse tokha.


Munthu aliyense asafunefune zokomera iye yekha, koma zokomeranso ena.


Ndani ali wofowoka, ine wosakhala naye mʼkufowoka kwakeko? Ndani amene mnzake amuchimwitsa, ine wosavutika mu mtima?


Ife sitikuyika chokhumudwitsa pa njira ya wina aliyense, kuti utumiki wathu usanyozeke.


Pakuti aliyense amangofuna zokomera iye yekha osati zokomera Yesu Khristu.


Ngati musungadi lamulo laufumu lija lopezeka mʼMalemba lakuti, “Konda mnansi wako monga iwe mwini,” ndiye kuti mukuchita bwino.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa