2 Samueli 7:13 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero13 Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya. Onani mutuwoBuku Lopatulika13 Iye adzamangira dzina langa nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa chimpando cha ufumu wake ku nthawi zonse. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 201413 Iye adzamangira dzina langa nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa chimpando cha ufumu wake ku nthawi zonse. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa13 Iyeyo ndiye adzandimangire Nyumba yomveketsa dzina langa, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake kuti ukhale wamuyaya. Onani mutuwo |
Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pa mpando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi.