Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




2 Samueli 24:7 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

7 Kenaka iwo anapita molunjika linga la ku Turo ndi ku mizinda yonse ya Ahivi ndi Akanaani. Pomaliza anapita ku Beeriseba ku Negevi wa ku Yuda.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

7 nafika ku linga la Tiro ndi kumizinda yonse ya Ahivi ndi ya Akanani; natulukira kumwera kwa Yuda ku Beereseba.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

7 nafika ku linga la Tiro ndi kumidzi yonse ya Ahivi ndi ya Akanani; natulukira kumwera kwa Yuda ku Beereseba.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

7 Ndipo adakafika ku linga la Tiro ndi ku mizinda yonse ya Ahivi, ndi ya Akanani. Atatero, adachoka kumeneko nakafika kumwera kwa Yuda, ku Beereseba.

Onani mutuwo Koperani




2 Samueli 24:7
10 Mawu Ofanana  

Choncho mfumu inati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali nawo. “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba kuti mukawerenge anthu omenya nkhondo ndi cholinga choti ndidziwe chiwerengero chawo.”


Atayendayenda mʼdziko lonse anabwerera ku Yerusalemu patapita miyezi isanu ndi inayi ndi masiku makumi awiri.


Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.


Inatumizanso uthenga kwa Akanaani amene ankakhala kummawa ndi kumadzulo kwa Yorodani. Uthenga unapitanso kwa Aamori, Ahiti, Aperezi ndi Ayebusi amene amakhala mʼdziko la ku mapiri ndiponso kwa Ahivi amene ankakhala mʼmunsi mwa phiri la Herimoni ku chigwa cha Mizipa.


Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.


Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,


Mafumu onse okhala kumadzulo kwa Yorodani atamva zimenezi pamodzi ndi mafumu okhala ku mayiko a ku mapiri, mu zigwa, mʼmbali mwa Nyanja yayikulu mpaka ku Lebanoni (mafumu a Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi, ndi Ayebusi),


Koma Aisraeli anayankha Ahiviwo kuti, “Mwinatu inu mukukhala pafupi ndi ife. Tsono ife tingachite bwanji mgwirizano ndi inu?”


Mitundu ya anthuyo ndi: Mafumu asanu a Afilisti, Akanaani onse, Asidoni, ndi Ahivi amene ankakhala ku mapiri a Lebanoni kuyambira ku phiri la Baala-Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa