Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




2 Samueli 24:5 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Atawoloka Yorodani, iwo anamanga misasa yawo pafupi ndi Aroeri kummwera kwa mzinda wa ku chigwa ndipo kenaka iwo anapita ku dziko la Gadi mpaka ku Yazeri.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

5 Naoloka Yordani, namanga zithando ku Aroere ku dzanja lamanja kwa mzinda uli pakati pa chigwa cha Gadi, ndi ku Yazere;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Naoloka Yordani, namanga zithando ku Aroere ku dzanja lamanja kwa mudzi uli pakati pa chigwa cha Gadi, ndi ku Yazere;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Adaoloka mtsinje wa Yordani, nayambira ku Aroere, mzinda umene uli pakati pa chigwa cha ku Gadi, mpaka ku Yazere.

Onani mutuwo Koperani




2 Samueli 24:5
12 Mawu Ofanana  

Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu ndi atsogoleri a ankhondo. Choncho anachoka pamaso pa mfumu kupita kukawerenga anthu omenya nkhondo mu Israeli.


Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi popanda wina woziopseza.


Mose atatumiza azondi ku Yazeri, Aisraeliwo analanda midzi yozungulira ndi kuthamangitsa Aamori omwe ankakhala kumeneko.


Arubeni ndi Agadi amene anali ndi ngʼombe zambiri ndi ziweto zina anaona dziko la Yazeri ndi la Giliyadi kuti linali labwino kwa ziwetozo.


“Ataroti, Diboni, Yazeri, Nimira, Hesiboni, Eleali, Sebamu, Nebo ndi Beoni,


Atiroti-Sofani, Yazeri, Yogibeha,


Kuchokera ku Aroeri mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni ndi ku mzinda wa ku mtsinjeko mpaka kukafika ku Giliyadi, panalibe ndi mzinda ndi umodzi omwe umene unatikanika kuwugonjetsa. Yehova Mulungu wathu anatipatsa onsewo.


Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.


Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;


Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.


Aroeri, Sifimoti, Esitemowa


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa