Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




2 Samueli 19:1 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yowabu anawuzidwa kuti, “Mfumu ikulira maliro a Abisalomu.”

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

1 Ndipo anauza Yowabu, Onani mfumu ilikulira misozi, nilira Abisalomu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Ndipo anauza Yowabu, Onani mfumu ilikulira misozi, nilira Abisalomu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Anthu ena adauza Yowabu kuti, “Amfumutu akulira maliro a Abisalomu.”

Onani mutuwo Koperani




2 Samueli 19:1
9 Mawu Ofanana  

Ngakhale kuti ana ake onse aamuna ndi aakazi anasonkhana kudzamutonthoza, iye anakana kutonthozedwa. Iye anati, “Ayi. Ndidzalira mpaka ndidzapite kwa mwana wanga ku manda.” Choncho Israeli anapitirirabe kulira mwana wake.


Koma munthuyo anayankha kuti, “Ngakhale atandipatsa mʼmanja mwanga ndalama zasiliva 1,000, sindingatambasule dzanja langa kupha mwana wa mfumu. Ife tikumva, mfumu inalamula inu Abisai ndiponso Itai kuti, ‘Mutetezeni mnyamatayo Abisalomu chifukwa cha ine!’


Yowabu anati, “Ine sinditayanso nthawi ndi iwe.” Ndipo anatenga mikondo itatu mʼmanja mwake ndipo anabaya pamtima pa Abisalomu, Abisalomuyo akanali ndi moyo pa mtengo wa thundu.


Yowabu anamuwuza iye kuti, “Iwe si amene uti ukanene zimenezi lero. Ukapereka uthenga nthawi ina, koma usatero lero, chifukwa mwana wa mfumu wafa.”


Mfumu inanthunthumira. Inapita ku chipinda cha mmwamba cha pa chipata kukalira. Pamene imapita, inkati: “Iwe mwana wanga Abisalomu! Mwana wanga! Mwana wanga Abisalomu! Zikanakhala bwino ndikanafa ndine mʼmalo mwako! Iwe Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga!”


Mfumu inalamulira Yowabu, Abisai ndi Itai kuti, “Mumukomere mtima Abisalomu chifukwa cha ine.” Ndipo asilikali onse anamva pamene mfumu imalamula izi za Abisalomu kwa wolamulira aliyense.


Ndipo kwa asilikali onse chipambano cha tsiku limenelo chinasandulika maliro, chifukwa tsiku limenelo anthu anamva kuti mfumu ili pa chisoni chachikulu chifukwa cha mwana wake.


Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.


“Ndipo pa nyumba ya Davide ndi pa anthu okhala mu Yerusalemu ndidzakhuthulirapo mzimu wachisomo ndi wopemphera. Iwo adzandiyangʼana Ine, amene anamubaya, ndipo adzamulirira kwambiri monga momwe munthu amalirira mwana wake mmodzi yekhayo, ndiponso adzamva chisoni kwambiri monga momwe amachitira ndi mwana woyamba kubadwa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa