2 Samueli 10:12 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero12 Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.” Onani mutuwoBuku Lopatulika12 Ulimbike mtima, ndipo tichite chamuna lero chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu; Yehova nachite chomkomera. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 201412 Ulimbike mtima, ndipo tichite chamuna lero chifukwa cha anthu athu ndi midzi ya Mulungu wathu; Yehova nachite chomkomera. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa12 Limba mtima, ndipo tichite chamuna chifukwa cha anthu athu, ndiponso chifukwa cha mizinda ya Mulungu wathu. Chauta achite zimene zimkomere.” Onani mutuwo |
“Pitani, mukasonkhanitse pamodzi Ayuda onse amene ali mu Susa ndipo mundisalire chakudya. Musadye kapena kumwa kwa masiku atatu, usiku ndi usana. Ine ndi anamwali anga onditumikira tidzasala chakudya monga inu. Izi zikachitika, ine ndidzapita kwa mfumu, ngakhale kutero ndikutsutsana ndi lamulo. Ndipo ngati nʼkufa ndife ndithu.”