Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




2 Samueli 1:19 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

19 “Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

19 Ulemerero wako, Israele, unaphedwa pa misanje yako. Ha! Adagwa amphamvu!

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

19 Ulemerero wako, Israele, unaphedwa pa misanje yako. Ha! Adagwa amphamvu!

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

19 “Ulemerero wako wathera zitunda zako zachipembedzo, iwe Israele. Ha! Kani amphamvu agwa motere!

Onani mutuwo Koperani




2 Samueli 1:19
11 Mawu Ofanana  

“Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.


“Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.


“Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”


Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli.


Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.


Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni ndi mtambo wa mkwiyo wake! Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli kuchoka kumwamba. Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso popondapo mapazi ake.


Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!


Kenaka ndinatenga ndodo yanga yotchedwa Kukoma mtima ndi kuyithyola, kuphwanya pangano limene ndinachita ndi mitundu yonse ya anthu.


Choncho ine ndinadyetsa nkhosa zokaphedwa, makamaka nkhosa zoponderezedwa. Pamenepo ndinatenga ndodo ziwiri ndipo yoyamba ndinayitcha Kukoma mtima ndipo yachiwiri ndinayitcha Umodzi ndipo ndinadyetsa nkhosazo.


Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa anapeza Sauli ndi ana ake atatu atafa pa phiri la Gilibowa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa