Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




1 Samueli 26:4 - Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 iye anatumiza anthu okazonda ndipo anapeza kuti Sauli wafikadi ndithu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Lopatulika

4 Chifukwa chake Davide anatumiza ozonda, nazindikira kuti Saulo anabwera ndithu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Chifukwa chake Davide anatumiza ozonda, nazindikira kuti Saulo anabwera ndithu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 Davide adatuma anthu oti akazonde, ndipo adapezadi kuti Saulo wafika.

Onani mutuwo Koperani




1 Samueli 26:4
4 Mawu Ofanana  

“Taonani ndikukutumizani inu monga nkhosa pakati pa mimbulu. Chifukwa chake khalani ochenjera ngati njoka ndi woona mtima ngati nkhunda.


Tsono Yoswa mwana wa Nuni anatuma anthu awiri okazonda dziko mwachinsinsi kuchokera ku Sitimu. Iye anawawuza kuti, “Pitani mukaone dzikolo makamaka mzinda wa Yeriko.” Kotero iwo anapita ndipo anakafika ku nyumba ya mkazi wadama dzina lake Rahabe, ndipo anagona kumeneko.


Sauli anamanga msasa wake mʼmbali mwa njira yopita ku phiri la Hakila moyangʼanana ndi Yesimoni. Koma Davide anali mʼchipululumo. Davide ataona kuti Sauli amamulondola mpaka kumeneko,


Tsono Davide ananyamuka napita kumalo kumene Sauli anamanga misasa. Iye anaona pamene Sauli ndi Abineri mwana wa Neri mkulu wa ankhondo anagona. Sauli anagona mʼkati mwa tenti ndipo asilikali anagona momuzungulira.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa