Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yoswa 7:1 - Buku Lopatulika

1 Koma ana a Israele analakwa ndi choperekedwacho; popeza Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda, anatapa choperekedwacho; ndi mkwiyo wa Yehova unayakira ana a Israele.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Koma ana a Israele analakwa ndi choperekedwacho; popeza Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda, anatapa choperekedwacho; ndi mkwiyo wa Yehova unayakira ana a Israele.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Koma Aisraele ena sadamvere lamulo la Chauta loti asatenge kanthu kena kalikonse koyenera kuwonongedwa. Tsono amene adaagwinyako zinthuzo, anali Akani. Iyeyu anali mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda. Choncho Chauta adakwiyira Aisraele onse kwambiri.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Koma Aisraeli anachita zachinyengo ndi lamulo lija loti asatenge kalikonse koyenera kuwonongedwa. Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda anatengako zinthu zina. Choncho Yehova anakwiyira Israeli kwambiri.

Onani mutuwo Koperani




Yoswa 7:1
19 Mawu Ofanana  

Ndipo ana aamuna a Yakobo anadza kwa ophedwa nafunkha mzinda chifukwa anamuipitsa mlongo wao.


Ndipo mkwiyo wa Yehova unayakanso pa Israele, nafulumiza Davide pa iwo, nati, Muka, nuwerenge Israele ndi Yuda.


Ndipo pamene anafika kumsanje anazilandira m'manja mwao, naziika m'nyumba; nauza anthuwo amuke, iwo nachoka.


Ndipo Mulungu anaipidwa nacho chinthuchi, chifukwa chake Iye anakantha Israele.


Ndipo anasiya nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo ao, natumikira zifanizo, ndi mafano; ndipo mkwiyo unawagwera Yuda ndi Yerusalemu, chifukwa cha kupalamula kwao kumene.


ndipo ndinati, Mulungu wanga, ndigwa nkhope, ndi kuchita manyazi kuweramutsa nkhope yanga kwa inu Mulungu wanga, popeza mphulupulu zathu zachuluka pamutu pathu, ndi kupalamula kwathu kwakula kufikira mu Mwamba.


Choipa chanu chikhoza kuipira munthu wonga inu, ndi chilungamo chanu chikhoza kukomera wobadwa ndi munthu.


Nzeru ipambana zida za nkhondo; koma wochimwa mmodzi aononga zabwino zambiri.


Ambuye, chilungamo ncha Inu, koma kwa ife manyazi a nkhope yathu, monga lero lino; kwa anthu a Yuda, ndi kwa okhala mu Yerusalemu, ndi kwa Aisraele onse okhala pafupi ndi okhala kutali, kumaiko onse kumene mudawaingira, chifukwa cha kulakwa kwao anakulakwirani nako.


Ndipo Mose anati kwa Aroni, ndi kwa Eleazara ndi Itamara ana ake, Musawinda tsitsi, musang'amba zovala zanu; kuti mungafe, ndi kuti angakwiye Iye ndi khamu lonse; koma abale anu, mbumba yonse ya Israele, alire chifukwa cha motowu Yehova anauyatsa.


Ndipo anati yense kwa mnzake, Tiyeni tichite maere, kuti tidziwe choipa ichi chatigwera chifukwa cha yani. M'mwemo anachita maere, ndipo maere anagwera Yona.


Utero msonkhano wonse wa Yehova, Cholakwa ichi nchiyani mwalakwira nacho Mulungu wa Israele, ndi kumtembenukira Yehova lero lino kusamtsatanso, popeza munadzimangira guwa la nsembe kupikisana ndi Yehova lero lino?


kuti mubwerera lero lino kusatsata Yehova? Ndipo kudzakhala kuti popeza lero mupikisana ndi Yehova, mawa adzakwiyira gulu lonse la Israele.


Kodi Akani mwana wa Zera sanalakwe m'choperekedwacho, ndipo mkwiyo unagwera gulu lonse la Israele? Osangoonongeka yekha munthuyo mu mphulupulu yake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa