Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yoswa 5:7 - Buku Lopatulika

7 Koma ana ao aamuna amene anawautsa m'malo mwao, iwowa Yoswa anawadula; popeza anakhala osadulidwa, pakuti sanawadule panjira.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

7 Koma ana ao amuna amene anawautsa m'malo mwao, iwowa Yoswa anawadula; popeza anakhala osadulidwa, pakuti sanawadule panjira.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

7 Koma ana ao amene adaloŵa m'malo mwao, sadaumbalidwe pamene anali paulendo m'chipululumo, ndipo ndiwo amene Yoswa adalamula kuti aumbalidwe.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

7 Koma ana awo amene analowa mʼmalo mwawo ndiwo amene Yoswa anawachita mdulidwe popeza sanachite pamene anali pa ulendo wawo mʼchipululu muja.

Onani mutuwo Koperani




Yoswa 5:7
5 Mawu Ofanana  

nati kwa iwo, Sitingathe kuchita ichi, kupereka mlongo wathu kwa mwamuna wosadulidwa; chifukwa kumeneko ndiko kutichepetsa ife.


Koma makanda anu, amene munanena za iwowa kuti adzakhala chakudya, amenewo ndidzawalowetsa, ndipo adzadziwa dzikolo mudalikana.


Ndipo ana anu amene mudanena, Adzakhala ogulidwa, ndi ana anu osadziwa chabwino kapena choipa ndi pano, iwo adzalowamo, ndidzawapatsa iwo ili, adzalilandira ndi iwo.


Pakuti ana a Israele anayenda m'chipululu zaka makumi anai, mpaka mtundu wonse wa amuna ankhondo otuluka mu Ejipito udatha, chifukwa cha kusamvera mau a Yehova; ndiwo amene Yehova anawalumbirira kuti sadzawaonetsa dziko limene Yehova analumbirira makolo ao kudzatipatsa, ndilo dziko moyenda mkaka ndi uchi.


Ndipo kunali, atatha kudula mtundu wonse, anakhala m'malo mwao m'chigono mpaka adachira.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa