Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yoswa 5:5 - Buku Lopatulika

5 Pakuti anthu onse anatulukawo anadulidwa; koma anthu onse obadwa m'chipululu panjira potuluka mu Ejipito sanadulidwe.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Pakuti anthu onse anatulukawo anadulidwa; koma anthu onse obadwa m'chipululu panjira potuluka m'Ejipito sanadulidwe.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Anthu onse amene adaatuluka ku Ejipito anali ataumbalidwa kale, koma onse obadwira m'chipululu pa nthaŵi ya ulendo wofuma ku Ejipito anali osaumbalidwa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Anthu onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto anali atachita mwambo wa mdulidwe, koma onse amene anabadwira mʼchipululu, pa ulendo wochoka ku Igupto, sanachite.

Onani mutuwo Koperani




Yoswa 5:5
9 Mawu Ofanana  

Koma mukadadziwa nchiyani ichi, Ndifuna chifundo, si nsembe ai; simukadaweruza olakwa iwo osachimwa,


Chifukwa chake ngati wosadulidwa asunga zoikika za chilamulo, kodi kusadulidwa kwake sikudzayesedwa ngati mdulidwe?


Mdulidwe ulibe kanthu, ndi kusadulidwa kulibe kanthu, koma kusunga kwa malamulo a Mulungu.


Pakuti mwa Khristu Yesu kapena mdulidwe kapena kusadulidwa kulibe mphamvu; komatu chikhulupiriro, chakuchititsa mwa chikondi.


Pakuti mdulidwe ulibe kanthu, kusadulidwa kulibe kanthunso, komatu wolengedwa watsopano.


Koma chifukwa chakuti Yoswa anawadula ndi ichi: anthu onse otuluka mu Ejipito, anthu aamuna, ndiwo amuna onse ankhondo, adafa m'chipululu panjira, atatuluka mu Ejipito.


Pakuti ana a Israele anayenda m'chipululu zaka makumi anai, mpaka mtundu wonse wa amuna ankhondo otuluka mu Ejipito udatha, chifukwa cha kusamvera mau a Yehova; ndiwo amene Yehova anawalumbirira kuti sadzawaonetsa dziko limene Yehova analumbirira makolo ao kudzatipatsa, ndilo dziko moyenda mkaka ndi uchi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa