Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yoswa 20:4 - Buku Lopatulika

4 Munthu akathawira umodzi wa mizinda iyi, aziima polowera pa chipata cha mzindawo, nafotokozere mlandu wake m'makutu a akulu a mzindawo; pamenepo azimlandira kumzinda kwao, ndi kumpatsa malo, kuti akhale pakati pao.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Munthu akathawira umodzi wa midzi iyi, aziima polowera pa chipata cha mudziwo, nafotokozere mlandu wake m'makutu a akulu a mudziwo; pamenepo azimlandira kumudzi kwao, ndi kumpatsa malo, kuti akhale pakati pao.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 Angathe kuthaŵira ku umodzi mwa mizinda imeneyo, nakafika pa malo achiweruzo amene ali pa chipata cha mzindawo. Atafika, asimbire atsogoleri mlandu wakewo. Apo atsogoleriwo adzamlola kuloŵa mumzindamo, nadzampatsa malo oti azikhalako.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Ngati munthu wathawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi, akafike pa malo oweruzira milandu amene ali pa chipata cha mzindawo ndipo akafotokoze mlandu wake pamaso pa akuluakulu a mzindawo. Kenaka iwo adzamulola kulowa mu mzinda wawo ndi kumupatsa malo woti akhale nawo.

Onani mutuwo Koperani




Yoswa 20:4
8 Mawu Ofanana  

Muja ndinatuluka kunka kuchipata kumzinda, muja ndinakonza pokhala panga kukhwalala,


Ana ake akhala otekeseka, napsinjika kuchipata, wopanda wina wakuwapulumutsa.


Musandichotsere mzimu wanga pamodzi ndi olakwa, kapena moyo wanga pamodzi ndi anthu okhetsa mwazi;


Mwamuna wake adziwika kubwalo, pokhala pakati pa akulu a dziko.


Ndipo pamene Ebedemeleki Mkusi, mdindo, anamva kuti anamuika Yeremiya m'dzenje; mfumu ilikukhala pa Chipata cha Benjamini;


kuti mwa zinthu ziwiri zosasinthika, m'mene Mulungu sangathe kunama, tikakhale nacho chotichenjeza cholimba, ife amene tidathawira kuchigwira chiyembekezo choikika pamaso pathu;


Kuti athawireko wakupha munthu osamupha dala, osadziwa; ndipo idzakhalire inu yopulumukirako, kumpulumuka wolipsa mwazi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa