Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yoswa 2:10 - Buku Lopatulika

10 Popeza tidamva kuti Yehova anaphwetsa madzi a mu Nyanja Yofiira pamaso panu, muja mudatuluka mu Ejipito; ndi chija munachitira mafumu awiri a Aamori okhala tsidya la Yordani, ndiwo Sihoni ndi Ogi, amene mudawaononga konse.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Popeza tidamva kuti Yehova anaphwetsa madzi a m'Nyanja Yofiira pamaso panu, muja mudatuluka m'Ejipito; ndi chija munachitira mafumu awiri a Aamori okhala tsidya la Yordani, ndiwo Sihoni ndi Ogi, amene mudawaononga konse.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Inde, tamva m'mene Chauta adaphwetsera Nyanja Yofiira inu mukufika, m'mene munkatuluka ku Ejipito. Tamvanso m'mene mudakanthira mafumu aŵiri a Aamori, Sihoni ndi Ogi, kuvuma kwa Yordani kuja. Mudakantha ndi magulu ao ankhondo omwe.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Ife tinamva mmene Yehova anawumitsira madzi a Nyanja Yofiira inu mukufika pamene munatuluka mʼdziko la Igupto. Tamvanso zimene munachita kwa Sihoni ndi Ogi, mafumu awiri a Aamori amene ali kummawa kwa Yorodani. Inu munawawononga kotheratu.

Onani mutuwo Koperani




Yoswa 2:10
13 Mawu Ofanana  

Mudagawa kasupe ndi mtsinje; mudaphwetsa mitsinje yaikulu.


Pamenepo Mose anatumiza amithenga ochokera ku Kadesi kumuka kwa mfumu ya Edomu, ndi kuti, Atero mbale wanu Israele, Mudziwa zowawa zonse zinatigwera;


Mulungu awatulutsa mu Ejipito; mphamvu yake ikunga ya njati.


Mulungu amtulutsa mu Ejipito; ali nayo mphamvu yonga ya njati; adzawadya amitundu, ndiwo adani ake. Nadzamphwanya mafupa ao, ndi kuwapyoza ndi mivi yake.


Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanatilole kupitira kwao; popeza Yehova Mulungu wanu anaumitsa mzimu wake, nalimbitsa mtima wake, kuti ampereke m'dzanja lanu, monga lero lino.


Ndipo ndinatuma mavu atsogolere inu, amene anawaingitsa pamaso panu, ndiwo mafumu awiri a Aamori; osati ndi lupanga lako, kapena ndi uta wako ai.


kuti mitundu yonse ya padziko lapansi idziwe dzanja la Yehova, kuti ndilo lamphamvu; kuti iope Yehova Mulungu wanu masiku onse.


Ndipo kunali, pamene mafumu onse a Aamori okhala tsidya la kumadzulo la Yordani, ndi mafumu onse a Akanani okhala ku nyanja anamva kuti Yehova anaphwetsa madzi a Yordani pamaso pa ana a Israele mpaka titaoloka, mtima wao unasungunuka, analibenso moyo chifukwa cha ana a Israele.


ndi zonse anachitira mafumu awiri a Aamori okhala tsidya lija la Yordani, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni, ndi Ogi mfumu ya ku Basani wokhala ku Asitaroti.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa