Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yoswa 18:3 - Buku Lopatulika

3 Ndipo Yoswa anati kwa ana a Israele, Muchedwa mpaka liti kulowa ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu anakupatsani?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Ndipo Yoswa anati kwa ana a Israele, Muchedwa mpaka liti kulowa ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu anakupatsani?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Motero Yoswa adafunsa Aisraele kuti, “Kodi mudzadikira mpaka liti kuti muloŵe m'dziko limene Chauta, Mulungu wa makolo anu, adakupatsani?

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Ndipo Yoswa anati kwa Aisraeli, “Kodi mudikira mpaka liti kuti mulowe ndi kulanda dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani?

Onani mutuwo Koperani




Yoswa 18:3
15 Mawu Ofanana  

Wochita ndi dzanja laulesi amasauka; koma dzanja la akhama lilemeretsa.


Moyo wa waulesi ukhumba osalandira kanthu; koma moyo wa akhama udzalemera.


Mayendedwe a waulesi akunga linga laminga, koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.


Chilichonse dzanja lako lichipeza kuchichita, uchichite ndi mphamvu yako; pakuti mulibe ntchito ngakhale kulingirira ngakhale kudziwa, ngakhale nzeru, kumanda ulikupitako.


Tsiku lomwelo adzati kwa Yerusalemu, Usaopa Ziyoni, manja anu asakhale olefuka.


Ndipo poyandikira madzulo anatuluka, napeza ena ataima; nanena kwa iwo, Mwaimiranji kuno dzuwa lonse chabe?


Gwirani ntchito si chifukwa cha chakudya chimene chitayika koma cha chakudya chimene chitsalira kumoyo wosatha, chimene Mwana wa Munthu adzakupatsani inu; pakuti ameneyo Atate, ndiye Mulungu, adamlembera chizindikiro.


Khala wamphamvu, nulimbike mtima, pakuti udzagawira anthu awa dzikoli likhale cholowa chao, ndilo limene ndinalumbirira makolo ao kuwapatsa.


Ndipo Yoswa anakalamba, wa zaka zambiri; ndipo Yehova ananena naye, Wakalamba, wa zaka zambiri, ndipo latsala dziko lalikulukulu, alilandire cholowa chao.


Ndipo anatsala mwa ana a Israele mafuko asanu ndi awiri osawagawira cholowa chao.


Mudzifunire amuna, fuko lililonse amuna atatu; kuti ndiwatume, anyamuke, nayendeyende iwo pakati padziko, nalilembe monga mwa cholowa chao; nabwerenso kwa ine.


Nati iwo, Taukani, tiwakwerere; pakuti tapenya dziko, ndipo taonani, ndilo lokoma ndithu; ndi inu muli chete kodi? Musamachita ulesi kumuka ndi kulowa kulandira dzikolo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa