Yoswa 18:1 - Buku Lopatulika1 Ndipo msonkhano wonse wa ana a Israele unasonkhana ku Silo, nuutsa komweko chihema chokomanako; ndipo dziko linawagonjera. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20141 Ndipo msonkhano wonse wa ana a Israele unasonkhana ku Silo, nuutsa komweko chihema chokomanako; ndipo dziko linawagonjera. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa1 Ataligonjetsa dziko lonselo, Aisraele onse adasonkhana ku Silo, ndipo adamangako chihema chamsonkhano. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero1 Atagonjetsa dziko lonse Aisraeli anasonkhana ku Silo ndipo anayimikako tenti ya msonkhano. Onani mutuwo |
Koma mukayesa dziko la cholowa chanu nchodetsa, olokani kulowa m'dziko la cholowa cha Yehova m'mene chihema cha Yehova chikhalamo, nimukhale nacho cholowa pakati pa ife; koma musapikisana ndi Yehova kapena kupikisana nafe, ndi kudzimangira nokha guwa la nsembe, pamodzi ndi guwa la nsembe la Yehova Mulungu wathu.