Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yoswa 13:9 - Buku Lopatulika

9 kuyambira pa Aroere, wokhala m'mphepete mwa chigwa cha Arinoni, ndi mzinda uli pakati pa chigwa, ndi chidikha chonse cha Medeba mpaka ku Diboni;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

9 kuyambira pa Aroere, wokhala m'mphepete mwa chigwa cha Arinoni, ndi mudzi uli pakati pa chigwa, ndi chidikha chonse cha Medeba mpaka ku Diboni;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

9 Dziko laolo lidayambira ku Aroere, mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso ku mzinda wokhala pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikiza dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba kukafika ku Diboni.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

9 Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.

Onani mutuwo Koperani




Yoswa 13:9
15 Mawu Ofanana  

Naoloka Yordani, namanga zithando ku Aroere ku dzanja lamanja kwa mzinda uli pakati pa chigwa cha Gadi, ndi ku Yazere;


Momwemo anadzilembera magaleta zikwi makumi atatu mphambu ziwiri, ndi mfumu ya Maaka ndi anthu ake; nadza iwo, namanga misasa chakuno cha Medeba. Ana a Amoni omwe anasonkhana m'mizinda mwao, nadza kunkhondo.


Ndi ana ena a Yuda anakhala m'midzi ya kuminda yao, mu Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ndi mu Diboni ndi midzi yake, ndi mu Yekabizeele ndi midzi yake,


Akwera ku Kachisi, ndi ku Diboni, kumisanje, kukalira; pa Nebo ndi pa Medeba a Mowabu pali kulira; pamitu pao ponse pali dazi, ndevu zonse zametedwa.


Iwe mwana wamkazi wokhala mu Diboni, utsike pa ulemerero wako, nukhale ndi ludzu; pakuti wakufunkha Mowabu wakukwerera, iwe waononga malinga ako.


ndi pa Diboni, ndi pa Nebo, ndi pa Betedibilataimu;


Ndipo wakufunkha adzafikira pa mizinda yonse, sudzapulumuka mzinda uliwonse; chigwa chomwe chidzasakazidwa, ndipo chidikha chidzaonongedwa; monga wanena Yehova.


Tinawagwetsa; Hesiboni waonongeka kufikira ku Diboni, ndipo tinawapululutsa kufikira ku Nofa. Ndiwo wakufikira ku Medeba.


Kuyambira ku Aroere, ndiko kumphepete kwa mtsinje wa Arinoni, ndi kumudzi wokhala kumtsinje kufikira ku Giliyadi, kunalibe mzinda wakutitalikira malinga ake; Yehova Mulungu wathu anapereka yonse pamaso pathu.


Ndipo dziko ili tinalilanda muja; kuyambira ku Aroere, wa ku mtsinje wa Arinoni, ndi dera lina la ku mapiri a Giliyadi, ndi mizinda yake, ndinapatsa Arubeni ndi Agadi.


Koma ndinapatsa Arubeni ndi Agadi kuyambira ku Giliyadi kufikira ku mtsinje wa Arinoni, pakati pa chigwa ndi malire ake, kufikira mtsinje wa Yaboki, ndiwo malire a ana a Amoni;


Sihoni mfumu ya Aamori wokhala mu Hesiboni, wochita ufumu kuyambira ku Aroere ndiwo m'mphepete mwa chigwa cha Arinoni, ndi pakati pa chigwa ndi pa Giliyadi wogawika pakati, kufikira mtsinje wa Yaboki, ndiwo malire a ana a Amoni;


ndi mizinda yonse ya Sihoni mfumu ya Aamori, wakuchita ufumu mu Hesiboni, mpaka malire a ana a Amoni;


Malire ao anayambira ku Aroere wokhala m'mphepete mwa chigwa cha Arinoni, ndi mzinda uli pakati pa chigwa ndi chidikha chonse cha ku Medeba;


Pamodzi ndi iye Arubeni ndi Agadi analandira cholowa chao, chimene Mose adawapatsa tsidya ilo la Yordani kum'mawa, monga Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa