Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yoswa 10:10 - Buku Lopatulika

10 Ndipo Yehova anawamwaza pamaso pa Israele, ndipo anawakantha makanthidwe aakulu ku Gibiyoni, nawapirikitsa panjira yokwera pa Betehoroni, nawakantha mpaka Azeka, ndi mpaka Makeda.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Ndipo Yehova anawamwaza pamaso pa Israele, ndipo anawakantha makanthidwe akulu ku Gibiyoni, nawapirikitsa pa njira yokwera pa Betehoroni, nawakantha mpaka Azeka, ndi mpaka Makeda.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Chauta adaŵachititsa mantha adaniwo pamene adangoona nkhondo ya Aisraele ija. Motero Aisraele adapambana Aamori ku Gibiyoni, naŵathamangitsa kutsika phiri la ku Betehoroni ndi kuŵakantha mpaka ku Azeka ndi ku Makeda.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Yehova anachititsa mantha adani aja atangoona gulu lankhondo la Israeli. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamori ku Gibiyoni ndipo anawathamangitsa mu msewu wopita ku Beti-Horoni ndi kuwapha njira yonse yopita ku Azeka ndi Makeda.

Onani mutuwo Koperani




Yoswa 10:10
29 Mawu Ofanana  

Ndipo Iye anatumiza mivi, nawawaza; mphezi, nawaopsa.


Ndipo Solomoni anamanganso Gezere, ndi Betehoroni wakunsi,


Ndipo Yehova anakantha Akusi pamaso pa Asa ndi Yuda, nathawa Akusi.


Koma amuna a nkhondo amene Amaziya anawabwereretsa, kuti asamuke naye kunkhondo, anagwera mizinda ya Yuda kuyambira Samariya kufikira Betehoroni, nakantha a iwowa zikwi zitatu, nalanda zofunkha zambiri.


Ndipo anatuma mivi yake nawabalalitsa; inde mphezi zaunyinji, nawamwaza.


Pakuti sanalande dziko ndi lupanga lao, ndipo mkono wao sunawapulumutse. Koma dzanja lanu lamanja, ndi mkono wanu, ndi kuunika kwa nkhope yanu. Popeza munakondwera nao,


Pamene Wamphamvuyonse anabalalitsa mafumu m'dzikomo, munayera ngati matalala mu Zalimoni.


Ndipo anapirikitsa amitundu pamaso pao, nawagawira cholowa chao, ndi muyeso, nakhalitsa mafuko a Israele m'mahema mwao.


Pakuti Yehova adzauka monga m'phiri la Perazimu, nadzakwiya monga m'chigwa cha Gibiyoni; kuti agwire ntchito yake, ntchito yake yachilendo, ndi kuti achite chochita chake, chochita chake chachilendo.


Ndipo Yehova adzamveketsa mau ake a ulemerero, ndipo adzaonetsa kumenya kwa dzanja lake, ndi mkwiyo wake waukali, ndi lawi la moto wonyambita, ndi kuomba kwa mphepo, ndi mkuntho ndi matalala.


pamene nkhondo ya mfumu ya ku Babiloni inamenyana ndi Yerusalemu, ndi mizinda yonse ya Yuda imene inatsala, ndi Lakisi ndi Azeka; pakuti mizinda ya Yuda yamalinga yotsala ndi imeneyi.


Pamenepo Yehova adzatuluka, nadzachita nkhondo ndi amitundu aja, monga anachitira nkhondo tsiku lakudumana.


Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka pamaso panu, nadzawapirikitsa ndi kupirikitsa kwakukulu, kufikira ataonongeka.


Ndipo kunali, pakuthawa iwo pamaso pa Israele, potsikira pa Betehoroni, Yehova anawagwetsera miyala yaikulu yochokera kumwamba mpaka pa Azeka, nafa iwo; akufa ndi miyala yamatalala anachuluka ndi iwo amene ana a Israele anawapha ndi lupanga.


Ndipo Yoswa anagwira Makeda tsiku lomwe lija ndi kuukantha ndi lupanga lakuthwa, ndi mfumu yake yomwe; anawaononga konse, ndi amoyo onse anali m'mwemo, osasiyapo ndi mmodzi yense, nachitira mfumu ya ku Makeda monga anachitira mfumu ya ku Yeriko.


Ndipo Yoswa anawadzidzimukitsa; popeza anakwera kuchokera ku Giligala usiku wonse.


Ndipo Yehova anawapereka m'dzanja la Israele, ndipo anawakantha, nawapirikitsa mpaka ku Sidoni waukulu, ndi ku Misirefoti-Maimu, ndi ku chigwa cha Mizipa ku m'mawa; nawakantha mpaka sanawasiyire ndi mmodzi yense.


mfumu ya ku Makeda, imodzi; mfumu ya ku Betele, imodzi;


Yaramuti, ndi Adulamu, Soko, ndi Azeka;


ndi Gederoti, Betedagoni, ndi Naama, ndi Makeda; mizinda khumi ndi isanu ndi umodzi pamodzi ndi midzi yao.


natsikira kumadzulo kunka ku malire a Ayafileti, ku malire a Betehoroni wa kunsi, ndi ku Gezere; ndi matulukiro ake anali kunyanja.


Ndipo malire a ana a Efuremu, monga mwa mabanja ao, ndiwo: malire a cholowa chao kum'mawa ndiwo Ataroti-Adara, mpaka Betehoroni wa kumtunda;


ndi Kibizaimu ndi mabusa ake, Betehoroni ndi mabusa ake; mizinda inai.


Ndipo Yehova anaononga Sisera ndi magaleta onse ndi gulu lankhondo lonse, ndi lupanga lakuthwa pamaso pa Baraki; koma Sisera anatsika pagaleta nathawa choyenda pansi.


Koma Baraki anatsata magaleta ndi gululo mpaka Haroseti wa amitundu; ndi gulu lonse lankhondo la Sisera linagwa ndi lupanga lakuthwa, sanatsale munthu ndi mmodzi yense.


Nyenyezi zinathira nkhondo yochokera kumwamba, m'mipita mwao zinathirana ndi Sisera.


gulu lina linalowa njira yonka ku Betehoroni; ndi gulu linanso linalowa ku njira ya kumalire, akuyang'ana ku chigwa cha Zeboimu kuchipululuko.


Pamenepo Afilisti anasonkhanitsa makamu ao a nkhondo, naunjikana ku Soko wa ku Yuda, namanga zithando pakati pa Soko ndi Azeka ku Efesi-Damimu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa