Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yohane 6:50 - Buku Lopatulika

50 Mkate wotsika Kumwamba ndi uwu, kuti munthu akadyeko ndi kusamwalira.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

50 Mkate wotsika Kumwamba ndi uwu, kuti munthu akadyeko ndi kusamwalira.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

50 Koma chakudya chimene ndikunenachi ndi chimene chidatsika kuchokera Kumwamba, kuti munthu atachidya asafe.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

50 Koma pano pali chakudya chochokera kumwamba, chimene munthu akadya sangafe.

Onani mutuwo Koperani




Yohane 6:50
11 Mawu Ofanana  

Ndipo kulibe munthu anakwera Kumwamba, koma Iye wotsikayo kuchokera Kumwamba, ndiye Mwana wa Munthu, wokhala mu Mwambayo.


Iye amene akhulupirira Mwanayo ali nao moyo wosatha; koma iye amene sakhulupirira Mwanayo sadzaona moyo, koma mkwiyo wa Mulungu ukhala pa iye.


Indetu, indetu, ndinena kwa inu, kuti iye wakumva mau anga, ndi kukhulupirira Iye amene anandituma Ine, ali nao moyo wosatha, ndipo salowa m'kuweruza, koma wachokera kuimfa, nalowa m'moyo.


Pakuti mkate wa Mulungu ndiye wakutsika kuchokera Kumwamba ndi kupatsa moyo kwa dziko lapansi.


Ndipo iwo ananena, Si Yesu uyu, mwana wa Yosefe, atate wake ndi amai wake tiwadziwa? Anena bwanji tsopano, kuti, Ndinatsika Kumwamba?


Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Iye wokhulupirira ali nao moyo wosatha.


Mkate wamoyo wotsika Kumwamba Ndine amene. Ngati munthu wina akadyako mkate umene, adzakhala ndi moyo kosatha. Inde, ndipo mkate umene ndidzapatsa Ine, ndiwo thupi langa, ukhale moyo wa dziko lapansi.


Mkate wotsika Kumwamba ndi umenewu: si monga makolowo, anadya namwalira; iye wakudya mkate umene adzakhala ndi moyo nthawi zonse.


Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Munthu akasunga mau anga, sadzaona imfa nthawi yonse.


Ndipo ngati Khristu akhala mwa inu, thupilo ndithu lili lakufa chifukwa cha uchimo; koma mzimu uli wamoyo chifukwa cha chilungamo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa