Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yohane 14:15 - Buku Lopatulika

15 Ngati mukonda Ine, sungani malamulo anga.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

15 Ngati mukonda Ine, sungani malamulo anga.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

15 “Ngati mundikonda, muzidzatsata malamulo anga.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

15 “Ngati mundikonda Ine, sungani malamulo anga.

Onani mutuwo Koperani




Yohane 14:15
20 Mawu Ofanana  

Pakuti anaumirira Yehova osapatuka pambuyo pake, koma anasunga malamulo amene Yehova adawalamulira Mose.


Iye wakukonda atate wake, kapena amake koposa Ine, sayenera Ine, ndipo iye wakukonda mwana wake wamwamuna, kapena wamkazi koposa Ine, sayenera Ine.


Yesu anati kwa iwo, Mulungu akadakhala Atate wanu, mukadakonda Ine; pakuti Ine ndinatuluka, ndi kuchokera kwa Mulungu; pakuti sindinadze kwa Ine ndekha, koma Iyeyu anandituma Ine.


Ngati wina sakonda Ambuye, akhale wotembereredwa. Akudza Ambuye.


Pakuti mwa Khristu Yesu kapena mdulidwe kapena kusadulidwa kulibe mphamvu; komatu chikhulupiriro, chakuchititsa mwa chikondi.


Akhale nacho chisomo onse akukonda Ambuye wathu Yesu Khristu m'chosaonongeka.


amene mungakhale simunamuone mumkonda; amene mungakhale simumpenya tsopano, pokhulupirira, mukondwera naye ndi chimwemwe chosaneneka, ndi cha ulemerero:


Ndipo chikondi ndi ichi, kuti tiyende monga mwa malamulo ake. Ili ndi lamulolo, monga mudalimva kuyambira pachiyambi, kuti mukayende momwemo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa