Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yohane 11:35 - Buku Lopatulika

35 Yesu analira.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

35 Yesu analira.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

35 Yesu adayamba kulira.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

35 Yesu analira.

Onani mutuwo Koperani




Yohane 11:35
17 Mawu Ofanana  

Yosefe ndipo anafulumira, chifukwa mtima wake unakhumbitsa mphwake, ndipo anafuna polirira; nalowa m'chipinda chake naliramo.


Kodi sindinamlirire misozi wakulawa zowawa? Kodi moyo wanga sunachitire chisoni osowa?


Maso anga atsitsa mitsinje ya madzi, popeza sasamalira chilamulo chanu.


Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu; munthu wazisoni, ndi wodziwa zowawa; ndipo ananyozedwa monga munthu wombisira anthu nkhope zao; ndipo ife sitinamlemekeze.


M'mazunzo ao onse Iye anazunzidwa, ndipo mthenga wakuimirira pamaso pake anawapulumutsa; m'kukonda kwake ndi m'chisoni chake Iye anawaombola, nawabereka nawanyamula masiku onse akale.


Koma ngati simudzamva, moyo wanga udzalira m'tseri chifukwa cha kunyada kwanu; diso langa lidzalira kwambiri, lidzagwa misozi, chifukwa zoweta za Yehova zagwidwa m'nsinga.


Ndipo udzati kwa iwo mau awa, Maso anga agwe misozi usana ndi usiku, asaleke; pakuti namwali mwana wa anthu anga wasweka ndi kusweka kwakukulu, ndi bala lopweteka kwambiri.


Ha, mutu wanga ukadakhala madzi, ndi maso anga kasupe wa misozi, kuti usana ndi usiku ndilirire ophedwa a mwana wamkazi wa anthu anga!


Chifukwa cha zimenezi ndilira; diso langa, diso langatu likudza madzi: Pakuti wonditonthoza, wotsitsimutsa moyo wanga, anditalikira; ana anga asungulumwa, pakuti adaniwo apambana.


Ndipo pakumva izi iwo, Iye anaonjeza nanena fanizo, chifukwa anali Iye pafupi pa Yerusalemu, ndipo iwo anayesa kuti Ufumu wa Mulungu ukuti uonekere pomwepo.


Ndipo m'mene anayandikira, anaona mzindawo naulirira,


Pamenepo Yesu, pakumuona iye alikulira, ndi Ayuda akumperekeza iye alikulira, anadzuma mumzimu, navutika mwini,


nati, Mwamuika iye kuti? Ananena ndi Iye, Ambuye, tiyeni mukaone.


Pakuti sitili naye mkulu wa ansembe wosatha kumva chifundo ndi zofooka zathu; koma wayesedwa m'zonse monga momwe ife, koma wopanda uchimo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa